Home Politics Phungu waboma la Likoma a Christopher Ashems Songwe wati pali zokhoma zina zomwe zachititsa kuti munthawi yawo asakwanitse zina mwa zitukuko zomwe adalonjaza.

Phungu waboma la Likoma a Christopher Ashems Songwe wati pali zokhoma zina zomwe zachititsa kuti munthawi yawo asakwanitse zina mwa zitukuko zomwe adalonjaza.

by Chiletso Bisweck
0 comments

A Songwe anena izi lolemba pomwe anakonza mkumano wa adindo osiyanasiyana kuphatikizapo mafumu ndicholinga chowafotokozera zomwe achita kuchokera mchaka cha 2019.

“Munthawi yomwe ndakhala ndikukutumikilani ndakumana ndi zokhoma monga, kufowoka kwa akomiti oyang’anila ma polojekiti akudera, ma komiti a VDC ndi ADC kusalondoloza zitukuko, khonsolo kugula zipangizo zosayenera komanso kuchedwa kuyamba ntchito mwazina” anatero a Songwe.

Komabe phunguyu wati wakwanitsa ena mwa malonjezo ake mwachitsanzo, kubweletsa bwalo lamilandu, kuthetsa mavuto amagetsi, kumaliza zitukuko zimene zinayambidwa kale komanso kukhazikitsa thumba la ndalama zothandizila ana ovutika mu sukulu za sekondale.

Mkumanowu wachitika pomwe ma udindo a aphungu mdziko lino akhale akutha mwezi wa July chaka chino pokonzekela chisankho chapatatu chomwe chidzachitike pa 16 September.

Likomafm, online news.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00