Malingana ndi ofalitsa nkhani za Police ku Likoma sergeant Enala Kaluwa wati pawukadaulo wawo akwanitsa kugwira anthuwa ndipo onsewa akuyembekezeka kukawonekera kubwalo la mulandu posachedwapa pa mlandu opezeka ndi katundu wakuba.
Atatuwa ndi a Sunganani soko
azaka 31 am’mudzi wa Chioko, T.A Nkumpha boma Likoma. Nyangana Nyasulu azaka 32 am’mudzi wa Matandani, T.A Kamwandi boma la Nkhatabay, ndi a Chisomo Ganizani azaka 26 am’mudzi wa Kosamu, T.A Njombwa boma la Kasungu.
Kaluwa wati akwanitsanso kugwira m’modzi mwa anthu omwe amayendetsa bwato lomwe linanyamula anthuwa omwe anamila.