Home FeaturedFeatured Apolice M’boma la Likoma agwira abambo atatu ndikuwasunga muchitolokosi powaganizira mulandu wakuba komanso kupezeka ndi katundu wa anthu omwe anamira pangozi ya bwato yomwe inachitika loweluka sabata yapitayi m’bomali pomwe anthuwa amakakwera sitima ya MV Chilembwe.

Apolice M’boma la Likoma agwira abambo atatu ndikuwasunga muchitolokosi powaganizira mulandu wakuba komanso kupezeka ndi katundu wa anthu omwe anamira pangozi ya bwato yomwe inachitika loweluka sabata yapitayi m’bomali pomwe anthuwa amakakwera sitima ya MV Chilembwe.

by Oliver Malibisa
0 comments

Malingana ndi ofalitsa nkhani za Police ku Likoma sergeant Enala Kaluwa wati pawukadaulo wawo akwanitsa kugwira anthuwa ndipo onsewa akuyembekezeka kukawonekera kubwalo la mulandu posachedwapa pa mlandu opezeka ndi katundu wakuba.

Atatuwa ndi a Sunganani soko
azaka 31 am’mudzi wa Chioko, T.A Nkumpha boma Likoma. Nyangana Nyasulu azaka 32 am’mudzi wa Matandani, T.A Kamwandi boma la Nkhatabay, ndi a Chisomo Ganizani azaka 26 am’mudzi wa Kosamu, T.A Njombwa boma la Kasungu.

Kaluwa wati akwanitsanso kugwira m’modzi mwa anthu omwe amayendetsa bwato lomwe linanyamula anthuwa omwe anamila.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00