Home Sports Team ya Chiponde FC ndi akatswiri a FAM Cup Under 21 District League itagonjetsa Team ya Red Arrows 4-2.

Team ya Chiponde FC ndi akatswiri a FAM Cup Under 21 District League itagonjetsa Team ya Red Arrows 4-2.

by Oliver Malibisa
0 comments

Masewero omwe anachitikira pa Likoma Community Football ground la lamulungu anabweletsa kwimbi la anthu kuchokera m’madera onse aboma la Likoma ndipo anali masewero apamwamba.

M’mawu ake Mlembi wa mkulu wa bungwe loyendetsa masewero ku Likoma a Kondwani Binga ati chikho cha FAM Under 21 chawonetsa luso lomwe achanyamata achichepere alinalo, Iye watinso apeza kale zikho zina monga Castle Imbongetse, Christopher Ashems Songwe League, komanso FAM CUP zimene zikhale zikuyambanso posachedwapa chaka chino.

Captain wa Chiponde FC Benjamin Khuni wayamika bungweli pa ntchito yomwe akugwira yosaka thandizo kuti masewero ampira adzipita patsogolo m’bomali.

Naye Mike Gondwe yemwe ndi m’modzi mwa atsogoleri a team ya Red Arrows avomeleza kugonja kwawo ndipo ati mpikisano uliwonse amapambana ndi m’modzi.

Ma team okwana 14 ndiwomwe anatenga nawo mbali mu mpikisanowo, ndipo team ya Chiponde yapita ndi ndalama zokwana 1 miliyoni kwacha, pomwe team ya Red Arrows yatenga K400,000, pomwe Madimba yachoka ndi K200,000.

LikomaFM, Online News.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00