Home Featured Ofesi yowona za usodzi ku Likoma yati ndiyokondwa kuti tsopano asodzi ali ndi owaimira ku khonsolo.

Ofesi yowona za usodzi ku Likoma yati ndiyokondwa kuti tsopano asodzi ali ndi owaimira ku khonsolo.

by Chiletso Bisweck
0 comments

Mkulu woyendetsa ntchito za usodzi m’boma la Likoma, Lonjezo Chikopa wati tsopano pakhala posavuta kuti asodzi azitha kutula nkhawa zawo komanso kudziwa zomwe zikuchitika ku khonsolo kutsatila kusankhidwa kwa a Martin Mjima.

A Martin Mjima ati akonzeka kuimilira asodzi pomwe ati m’mbuyomu asodzi akhala akupangilidwa ziganizo popanda iwo eni.

“Tiyamikire khonsolo kamba kaganizoli poti m’mbuyomu tinalibe mpata oterewu,” anatero a Mjima.

Kupatula kukhala oyimira asodzi mnyumbayi a Mjima asankhidwanso kukhala mukomiti ya zaulimi ndi zachuma (Agriculture and finance).

Kusankhidwa kwa mnthumwiyi kukutsatila pempho la khansala wadera la kumwera kwa chilumba cha Likoma Ernest Travor Gulu yemwe anapeleka ganizoli posachedwapa.

LikomaFM, OnlineNews.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00