Home FeaturedFeatured Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

by Chiletso Bisweck
0 comments

Malingana ndi mneneri wa Police ya Likoma a Andrew Kusimbwa ati kumangidwaku kwachitika pambuyo pa ntchito yomwe inachitika ndi a polisiwa.

“A Banda atiuza kuti anamuuza mwanayo kuti awagwire kumaliseche kwawo, koma mwanayo anakana”

“Iwo akuti anachita zimenezi potsatira malangizo a sing’anga, pokhulupirira kuti mchitidwewu ungamupange kukhala wolemera”, watero Kusimbwa.

A Kusimbwa ati mwanayo anapulumutsidwa ndi amayi ake, omwe anapita kukamufunafuna ataona kuti sanabwerere kunyumba kutsatila kuyitanidwa ndi oganilizidwayu, ndipo amayiwa atafika kunyumba kwa a Banda anapeza zitseko zonse zotsekedwa koma anamva mawu a mwana wawo akufuula kuti athandizidwe.

A Charlse Banda amachokera m’mudzi wa mfumu Mtaya, T.A Mkhumpha m’boma la Likoma ali ndizaka 39 akawonekera kukhoti kuti akayankhe mlandu wochitala mwana zachipongwe.

LikomaFM, OnlineNews.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00