Malingana ndi kalata yomwe bungweri ladatulutsa pa 9 Julayi ndipo wasaina ndi mneneri wa bungweri a Sangwani Mwafulirwa yati mwambo otsegulira nyengo ya misonkhano ya kampeniyi udzachitikila mu mzinda wa Lilongwe.
Bungweri lati liyitana oyimila zipani, nthambi zaboma komanso mabungwe oyima pawokha mwa ena, ndipo apempha anthu onse kudzatsatira mwambowu kudzera mnyumba zowulutsa mau ndipo Likoma Community Radio idzakupatsilani tsatanetsatane wa mwambowu kuyambila 9 koloko m’mawa.
Pofika lero atsogoleri okwana 17 ndiwomwe awonetsa chidwi chodzapikisana nawo pampando wa President.
LikomaFM, Online News.