Home Featured Khonsolo ya Likoma yalandira ma Computer asanu othandizira sukulu ya Likoma community technical college kuchokera ku Bungwe la TEVETA.

Khonsolo ya Likoma yalandira ma Computer asanu othandizira sukulu ya Likoma community technical college kuchokera ku Bungwe la TEVETA.

by Chiletso Bisweck
0 comments

Polankhula lolemba pamwambo opeleka ma computer wa, mkulu woyendetsa ntchito za TEVETA m’chigawo chakumpoto a Joseph Chikopa ati ndicholinga chawo kuti Likoma Community technical college ikhale ndi ana omwe azisulidwa mwaukadaulo kotero apeleka ma Computer wa pofuna kuthandizira ntchito zina zapa sukuluyi

A Joseph apempha khonsolo ya Likoma kuwonetsetsa kuti zipangizozi zakusamalidwa ndicholinga chakuti pomwe mapulani ofuna kukuza sukuluyi ali mkati pasazakhalenso kusowekera zipangizozi.

M’mawu ake wapampando wakhonsoloyi khansala Justina Phiri wayamika bungwe la TEVETA kamba kathandizori, ponena kuti khonsolo payokha sakanatha kupedza ma Computer wa.

“Ndiwonetsetsa kuti katunduyi wapita ku Likoma Community technical college ndipo akugwira ntchito yake moyenera”, atero a Justina.

Likoma Community Technical College inayamba kugwira ntchito zake mchaka cha 2023 ndipo pakadali pano pali phunziro losoka lokha.

LikomaFM,OnlineNews.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00