Home FeaturedFeatured Khonsolo ya Likoma yati mwayi wa ntchito zosiyanasiyana ulipo mukhonsoloyi kwa achinyamata omwe ali ndi zowayeneleza.

Khonsolo ya Likoma yati mwayi wa ntchito zosiyanasiyana ulipo mukhonsoloyi kwa achinyamata omwe ali ndi zowayeneleza.

by Oliver Malibisa
0 comments

Poyankha funso la phungu wa Likoma a Christopher Ashems Songwe lomwe anafunsa lachisanu pa mkumano wa Full Council lokhudza ndondomeko zakalembedwe ka ntchito pakhonsoloyi, a Banabas Sambamo omwe ndi wapampando wa khonsoloyi anati ndizosavuta kulemba ntchito achinyamata ochokera m’bomali chofunika ndikukhala ndizowayeneleza.

A Sambamo anapitiliza kunena kuti posachedwapa akhala akutulutsa chikalata cha mwayi wantchito za Umoyo komanso magawo ena ndipo panthawiyi alankhulana ndi bwana mkubwa wa Likoma kuti achinyamata aku Likoma adzakhale ndi mwayi olembedwa ntchito.

Wayimilira achinyamata ku khonsoloyi Macfallen Mafuta wati ndizoona kuti achinyamata ambiri amakhala kuti zowayeneleza alibe kotero iye wati apita kumakalabu kukalimbikitsana ndi anzake za nkhaniyi.

Likomafm, Onlinenews.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00