Home Lifestyle Ngati njira imodzi yochepetsa umbanda m’boma la Likoma Senior Chief Mkumpha yachititsa mkumano wa asodzi ochokela m’ma boma ena.

Ngati njira imodzi yochepetsa umbanda m’boma la Likoma Senior Chief Mkumpha yachititsa mkumano wa asodzi ochokela m’ma boma ena.

by Chiletso Bisweck
0 comments

Polankhula pamsonkhanowu a Mathews Mwela anati anayitanitsa mkumanowu pomwe asodzi ochokera m’maboma ena akupita ku Likoma kukachita usodzi komanso bizinesi, asodziwa akuchokela m’maboma a Mangochi, Salima, Nkhotakota, Kalonga ndi ena, zomwe zikubweletsa umbanda komanso unve ku Likoma.

“asodzi ambiri akubwera osadziwitsa mafumu zomwe zikupeleka chiopsezo ndipo anthu ambili amene akupezeka ndi milandu yakuba kuno ku Likoma ndiwochokela m’maboma ena.”

Senior Chief Mkumpha ati akhala akupangitsa mikumanoyi m’madooko onse, kuti asodzi omwe akuchokela m’maboma ena akhale mkaundula wa amfumu adera lomwe akukhala komanso akhale ndichimbudzi pamalo pomwe akugwilira ntchito yawo.

M’modzi mwa asodzi omwe anachokela m’boma la Mangochi a Piason Nyozani athokoza mfumuyi kaamba kokonza mkumanowu ndipo ati alemekeza ndondomekozi.

Mkumanowu unachitikila pa dooko la mfumu Chalunda komwe anthu ochuluka amafikilako.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00