Home Politics Phungu wa boma la Likoma a Christopher Ashems Songwe apeleka thandizo ku ofesi ya maphunziro m’bomali kuti lithandizile masewero osambila.

Phungu wa boma la Likoma a Christopher Ashems Songwe apeleka thandizo ku ofesi ya maphunziro m’bomali kuti lithandizile masewero osambila.

by Chiletso Bisweck
0 comments

Phunguyu wapeleka thandizo la ndalama zokwana 1,000,000.00-kwacha lachisanu kudzera ku ofesi ya za masewero, District Education Sports Officer (DESO).

Polandila thandizoli mkulu wa za maphunziro m’bomali a Zimulange Mhango ayamikila a Songwe kamba kathandizo lomwe apeleka panthawi yake, ndipo anawonjezera kuti aka sikoyamba kuti Phunguyu athandize pankhani za maphunziro ndi ndalama za m’thumba mwawo, “ulendo wina anathandizira Quiz Competition komanso anyamata omwe ankapita ku mpikisano wa MASSA”, anatero a Mhango.

A Songwe ati ndi khumbo lawo kuona masewero osiyanasiyana akupita patsogolo kudzera m’masukulu chifukwa akudziwa bwino lomwe kuti ana ambiri luso lowe limaonekela akakhala ali pa sukulu, ndipo ati ndichiyembekezo chawo kuti thandizoli ligwira ntchito moyenera.

Thandizoli ladza pomwe ana asanu ndi mmodzi akuyembekezeka kupita ku maiko a Namibia ndi Algeria posachedwapa.

LikomaFM, OnlineNews.

You may also like

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00