Home Politics Yemwe adzapikisane nawo pampando wa ukhansala muwodi ya Chizumulu North m’boma la Likoma ati ndiwokonzeka kutumikila anthu akuderali.

Yemwe adzapikisane nawo pampando wa ukhansala muwodi ya Chizumulu North m’boma la Likoma ati ndiwokonzeka kutumikila anthu akuderali.

by Chiletso Bisweck
1 comment

A Andrew Zex Msalowa omwe adzayimile chipani cha Malawi Congress Party MCP, anena izi lero pa Chizumulu Community ground pomwe amakhazikitsa mfundo zawo zokopera anthu kuti adzawasankhe pachisankho chapa 16 September.

A Msalowa akuti anthu akadzawasankha iwo kukhala khansala wadelali adzapititsa patsogolo ntchito zaumoyo, zamaphunziro komanso zamasewero mwazina.

Potsegulira msonkhanowu mdera lachiteko amfumu a Chingole ati ndale simkangano kapena kunyozana ndipo ati atsogoleri omwe akupikisana pamipando yosiyanasiyana ndiwolandilidwa mdelali posatengera chipani.

Polankhulapo wapampando wa amayi kuchigawochi a Grace Mhone apempha anthu kudzavotere a Msalowa kaamba kakuti anayamba kale kupanga zitukuko monga kuthandizila chipatala cha Chiteko under 5 clinic ndi matumba a cement komanso lime mwazina.

LikomaFM, OnlineNews.

You may also like

1 comment

Coraline2335 August 5, 2025 - 1:27 am Reply

Leave a Comment

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00