Home Politics A Charles Chilambula omwe adzapikisane nawo pa mpando waphungu wa nyumba yamalamulo ku Likoma ati apitiliza kuchititsa misonkhano yokopa anthu kuti adzapambane pa chisankho chapa 16 September.

A Charles Chilambula omwe adzapikisane nawo pa mpando waphungu wa nyumba yamalamulo ku Likoma ati apitiliza kuchititsa misonkhano yokopa anthu kuti adzapambane pa chisankho chapa 16 September.

by Chiletso Bisweck
17 comments

A Chilambula alankhula izi lero atamaliza kupereka zikalata zawo zowayeneleza kudzapikisana nawo pachisankho chapa 16 September ngati mphungu pansi pa chipani cha Democratic Progressive Party.

“Ndine okondwa kuti ndaloledwa kudzapikisana nawo ngati phungu wa Likoma-Chizumulu Constituency choncho ndikuwapempha omwe analembetsa kuti akavote mwanzeru kuti Likoma wathu apite patsogolo.”

Naye mkulu okopa anthu mchipanichi a Farai Holland ati zatelemu apitiliza kumema anthu okhala m’boma la Likoma kuti adzavotere a Charles Chilambula,

“Nthawi zambiri kulikoma kuno timavotera anthu omwe ndi akuno koma sakhala kuno ndipo amangotiyendera ngati akudzazonda odwala ndikumapita, kulikoma timavutika nkhani yakudula kwa zakudya monga Chimanga, Sugar, ndi mitengo yakuchigayo mwazina koma pa 16 September pano mavuto onsewa akutha.” Atero a Holland.

Pakadali pano bungwe la Malawi Electral Commission, MEC lavomeleza anthu okwana anayi kuti ndiwoyenera kudzapikisana pampando waphungu ku Likoma Constituency, anayiwa ndi a Masauko Thawe oyima pawokha, a Christopher Ashems Songwe a Malawi CongressParty, a Vincent Chirwa a People’s Party, komanso a Charles Chilambula a Democratic Progressive Party.

LikomaFM, OnlineNews.

You may also like

17 comments

Damon4316 August 5, 2025 - 1:26 am Reply
Jane3729 August 13, 2025 - 5:05 pm Reply
Isabel3910 August 16, 2025 - 1:54 am Reply
Sylvia3610 August 16, 2025 - 3:53 pm Reply
Madison451 August 17, 2025 - 10:11 pm Reply
Justin855 August 19, 2025 - 2:55 am Reply
Lynn3175 August 20, 2025 - 4:56 am Reply
Felix3472 August 29, 2025 - 11:42 am Reply
Alastair2958 September 1, 2025 - 3:27 pm Reply
Jill3568 September 5, 2025 - 1:05 pm Reply
William3754 September 8, 2025 - 9:14 am Reply
Vanessa1428 September 10, 2025 - 5:16 am Reply
Leonard4023 September 18, 2025 - 10:25 am Reply
Martin706 October 9, 2025 - 8:08 am Reply
Emmett930 October 14, 2025 - 1:37 am Reply
Cole1724 October 22, 2025 - 8:54 am Reply
Donna997 December 2, 2025 - 5:53 am Reply

Leave a Reply to Martin706 Cancel Reply

Likoma (LCR) is a community radio for Likoma District licensed by
Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) in December
2013.The Radio is covering the whole of Likoma District including
Chizumulu, parts of Nkhata Bay,Mzuzu and Nkhotakota. The radio
station enjoys a listenership of about 50,000 comprising of 17,000 from
the island and others from Nkhata Bay, Nkhotakota and some parts
of Mozambique.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00