A Philip Chika Chilambula omwe anagonja pachisankho chachipulura pa mpando wa ukhansala mchipani cha Democratic Progressive Party DPP, akuti adzapikisana nawo pampandowo ngati oyima pawokha.

A Chilambula alankhula ndi Likoma radio kuti sanali okhutila ndi chisankho chomwe chinachitika mwezi wa Epulu ndipo ati anthu asamakopeke ndi ndalama koma mfundo.

“takhala tikuyenda pagalawundi ndichimene chandipatsa chitsimikizo kuti kuthekera kutha kupezeka ngati titapanga bwino kampeni”, atero a Philip.

Pakadali pano achilambula akuti chilichonse chofunika kuti adzapikisane nawo apanga kale kuphatikizapo kutenga zipepala ku ofesi ya MEC komanso kupeleka ndalama.

Zatelemu anthu okwana asanu ndiwomwe awonetsa chidwi chodzapikisana pa mpando wa ukhansala mchigawo chakumwela kwa chilumba cha Likoma.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

A Charles Chilambula omwe adzapikisane nawo pa mpando waphungu wa nyumba yamalamulo ku Likoma ati apitiliza kuchititsa misonkhano yokopa anthu kuti adzapambane pa chisankho chapa 16 September.

Yemwe adzapikisane nawo pampando wa ukhansala muwodi ya Chizumulu North m’boma la Likoma ati ndiwokonzeka kutumikila anthu akuderali.

Phungu wa boma la Likoma a Christopher Ashems Songwe apeleka thandizo ku ofesi ya maphunziro m’bomali kuti lithandizile masewero osambila.