Izi zadziwika pa mkumano omwe phungu wanyumba ya malamulo wa Likoma a Christopher Ashems Songwe anayitanitsa adindo osiyanasiyana kuphatikizapo mafumu lero pomwe amapeleka malipoti ake amomwe ntchito za chitukuko zayendera m’bomali kuyambila chaka cha 2019 mpaka 2025.
T.A Kabuthu wa chilumba cha Chizumulu wati zosemphana zomwe zinalipo zokhudza malo omwe jitiyi idzamangidwe zatha tsopano.
Enala Phiri yemwe ndi ochita malonda pa chilumbachi wati amayi ndi achikulire ndiwomwe akuvutika pokwera Sitima ndipo ndipo wati ganizo lopitiliza ntchitoyi ndiyopindulira anthu apachilumbachi
Naye wachinyamata ochokera m’dera la Chiteko pachilumbachi macfallen Mafuta ati ndizoona kuti pakali pano kusemphanaku kunatha ndipo boma lipitilize ndi ganizoli.