Gulu la Taskforce lomwe ndi nthambi ya chipani cha Malawi Congress Party m’boma la Likoma lapeleka Cement kuti amalizile nyumba ya chigayo.

Polankhula lachinayi pamwambo opeleka cement ku komiti yoyendetsa chigayochi, a Innocent Aponda omwe ndi mmodzi mwa guluri ati achita chidwi powona momwe phungu wa Likoma a Christopher Ashems Songwe akuchita pa nkhani ya zitukuko pomwe apeleka zigayo ziwiri dera la Chiponde ndi Chinyanya zomwe azigula ndi ndalama za mthumba mwawo.

Mlembi wakomiti ya chigayochi a Edward Chirwa ayamikira guluri kamba kathandizoli ndipo ati akonza kale ndondomeko yakayendetsedwe kantchitoyi ndipo mwazina ndikuzathandiza osowa, kulipilira feez komanso kukonzera zitukuko zina mdelari.

Mfumu yadelari Group Village Headman Mwase yathokoza a Joe Noel Chilala omwe azayimire delari ngati khansala kamba kosaka thandizoli.

Guluri lapereka matumba okwana khumi.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

A Charles Chilambula omwe adzapikisane nawo pa mpando waphungu wa nyumba yamalamulo ku Likoma ati apitiliza kuchititsa misonkhano yokopa anthu kuti adzapambane pa chisankho chapa 16 September.

Yemwe adzapikisane nawo pampando wa ukhansala muwodi ya Chizumulu North m’boma la Likoma ati ndiwokonzeka kutumikila anthu akuderali.

A Philip Chika Chilambula omwe anagonja pachisankho chachipulura pa mpando wa ukhansala mchipani cha Democratic Progressive Party DPP, akuti adzapikisana nawo pampandowo ngati oyima pawokha.