Bishop wa Anglican Dioceses of Northern Malawi wati mpingo uli ndi udindo waukulu potengapo mbali pachitukuko chadziko lino.

Rt.Rev. Fanuel Magangani wanena izi lamulungu lapitali pa St Peters Anglican Cathedral m’boma la likoma pamwambo osangalalira kuti Dioceses yi yakwanitsa zaka 30 ikutumikila.

Amagangani anati mpingo ukuyenela kukhala odzidalira pawokha pachuma osati kumangodali maiko akunja. “kale ngakhale zovala za usembe tinkadalira maiko akunja koma pakadali pano takula chifukwa tikudzipangila tokha”.

Ndipo awonjeza kuti pomwe Dioceses yi yakwanitsa zaka 30 ndiwosangalala kuti yakwanitsa kumanga sukulu komanso zipatala mdziko lino.

Nduna yawona za chitetezo cha mdziko a Ezekiel Ching’oma womwe anali mlendo olemekezeka pamwambowu m’malo mwa president wadziko lino anati boma la Dr Lazarus Chakwela limalimbikitsa kuti mipingo idzigwira ntchito limodzi ndi boma pachitukuko ndipo ndiwokondwa kuti mpingowo ukugwila ntchito yotamandika mdziko.

Dr Lazarus Chakwela wathandiza Dioceses yi ndi ndalama zokwana 10,000,000.00 kwacha, pomwe a Ezekiel Ching’oma anapeleka 5,000,000.00.

LikomaFM, Onlinenews.

Related posts

Khonsolo ya Likoma yalandira ma Computer asanu othandizira sukulu ya Likoma community technical college kuchokera ku Bungwe la TEVETA.

Khansala Justina Phiri wa chigawo chakumpoto kwa Chilumba cha Chizumulu ndiyemwe wasankhidwa kukhala Wapampando wa Khonsolo ya Likoma.

10 comments

Adriana3910 August 6, 2025 - 4:30 pm
Vincent1893 August 8, 2025 - 3:20 pm
Frida1437 August 10, 2025 - 2:37 am
Naomi91 August 10, 2025 - 5:51 pm
Jenny4569 August 13, 2025 - 8:39 am
Samantha3545 August 13, 2025 - 1:14 pm
Andre3040 August 14, 2025 - 10:15 am
Krista4305 August 15, 2025 - 1:23 pm
Harper3530 August 15, 2025 - 8:21 pm
Brielle1086 August 15, 2025 - 11:16 pm
Add Comment