Gulu la Tilerane la m’mudzi wa mfumu Mani M’boma la Likoma lathandiza mabanja awiri osowa ndikatundu ogonera.

Polankhula loweluka pamwambo opeleka katundu kumabanjawa, Wapampando wa Guluri mayi Gladies Njakale ati cholinga chaguluri ndikuonetsetsa kuti anthu akukhala moyo wopanda nkhawa, iwo atinso kuonjezera pakatundu yemwe apeleka lero gulu lawo lipitiliza kugwira ntchito zachifundozi.

Mayi Janet Boma azaka 62 am’mudzi wa mfumu Chilongola mdera la Khuyu omwe apindula ndi thandizori ayamikira gulu la Tilerane chifukwa chathandizoli, ndipo ati ngati nkotheka gululi likachitirenso ena.

Nawo mayi Edina Pitala azaka 83 a m’mudzi wa mfumu Mwase ayamikila gululi ndipo ati thandizoli labwela munthawi yake pomwe tili munyengo yozizira.

Gululi lapeleka bulangete, matres, komanso pilo kwawina aliyense kumabanja awiriwa

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

Kampani ya China Civil Engineering Construction kudzera mu unduna wa za mtengatenga ndi mtokoma yapereka ma life jacket 250 ku boma la Likoma.

Wapampando wa khonsolo ya boma la Likoma wati anthu omwe amapindula ndi porogalamu ya mtukula pakhomo adzigwilitsa moyenera ndalama zomwe amalandila mu porogalamuyi.

Chiponde Beach Resort yakonza mwambo wapadera pofuna kubweletsa pamodzi anthu ochita malonda m’boma la Likoma.