Mkulu woyang’anira nkhani za katemera wa Polio mdziko muno, a Blessing Nyirongo ati ali ndi chikhulupiliro kuti kampeni yopeleka katemera wamatendawa m’boma la Likoma ikhala yopambana.

A Nyirongo awuza Likoma Radio kuti kupeleka katemelayu kwatengera kupezeka kwa Polio munzinda wa Blantyre kotero a zaumoyo akangalika kupeleka katemelayu komanso kufalitsa mauthenga akuopsa kwa Polio.

Polankhulapo ofalitsa nkhani zaumoyo m’bomali a Adamson Chunga ati ana omwe amalandila katemelayu amakhala otetezeka ku matendawa.

A Chunda ati pali chiyembekezo kuti ntchito yopeleka katemelayu idzayambe pa 24 mpaka pa 27 March 2026, ndipo ana 3644 osaposera zaka khumi zakubadwa ndiwomwe akuyembezeka kulandira katemelayu.

LikomaFM,OnlineNews.

Related posts

Wamkulu wa kampani ya Malawi Lake Services wati kukweza mitengo kwa sitima ya MV Ilala kupititsa patsogolo ntchito za kampaniyi.

Ofesi yowona za usodzi ku Likoma yati ndiyokondwa kuti tsopano asodzi ali ndi owaimira ku khonsolo.

Wapampando oyang’anila chitukuko chadera la kumwera kwa chilumba cha Likoma a Anson Putaputa ati akusowekera maphunziro kuti ayambe kugwira ntchito yawo mwaukadaulo.