Phungu wa boma la Likoma a Christopher Ashems Songwe apeleka thandizo ku ofesi ya maphunziro m’bomali kuti lithandizile masewero osambila.

Phunguyu wapeleka thandizo la ndalama zokwana 1,000,000.00-kwacha lachisanu kudzera ku ofesi ya za masewero, District Education Sports Officer (DESO).

Polandila thandizoli mkulu wa za maphunziro m’bomali a Zimulange Mhango ayamikila a Songwe kamba kathandizo lomwe apeleka panthawi yake, ndipo anawonjezera kuti aka sikoyamba kuti Phunguyu athandize pankhani za maphunziro ndi ndalama za m’thumba mwawo, “ulendo wina anathandizira Quiz Competition komanso anyamata omwe ankapita ku mpikisano wa MASSA”, anatero a Mhango.

A Songwe ati ndi khumbo lawo kuona masewero osiyanasiyana akupita patsogolo kudzera m’masukulu chifukwa akudziwa bwino lomwe kuti ana ambiri luso lowe limaonekela akakhala ali pa sukulu, ndipo ati ndichiyembekezo chawo kuti thandizoli ligwira ntchito moyenera.

Thandizoli ladza pomwe ana asanu ndi mmodzi akuyembekezeka kupita ku maiko a Namibia ndi Algeria posachedwapa.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

A Charles Chilambula omwe adzapikisane nawo pa mpando waphungu wa nyumba yamalamulo ku Likoma ati apitiliza kuchititsa misonkhano yokopa anthu kuti adzapambane pa chisankho chapa 16 September.

Yemwe adzapikisane nawo pampando wa ukhansala muwodi ya Chizumulu North m’boma la Likoma ati ndiwokonzeka kutumikila anthu akuderali.

A Philip Chika Chilambula omwe anagonja pachisankho chachipulura pa mpando wa ukhansala mchipani cha Democratic Progressive Party DPP, akuti adzapikisana nawo pampandowo ngati oyima pawokha.