A Andrew Zex Msalowa omwe adzayimile chipani cha Malawi Congress Party MCP, anena izi lero pa Chizumulu Community ground pomwe amakhazikitsa mfundo zawo zokopera anthu kuti adzawasankhe pachisankho chapa 16 September.
A Msalowa akuti anthu akadzawasankha iwo kukhala khansala wadelali adzapititsa patsogolo ntchito zaumoyo, zamaphunziro komanso zamasewero mwazina.
Potsegulira msonkhanowu mdera lachiteko amfumu a Chingole ati ndale simkangano kapena kunyozana ndipo ati atsogoleri omwe akupikisana pamipando yosiyanasiyana ndiwolandilidwa mdelali posatengera chipani.
Polankhulapo wapampando wa amayi kuchigawochi a Grace Mhone apempha anthu kudzavotere a Msalowa kaamba kakuti anayamba kale kupanga zitukuko monga kuthandizila chipatala cha Chiteko under 5 clinic ndi matumba a cement komanso lime mwazina.
LikomaFM, OnlineNews.
1 comment