Chiponde Beach Resort yakonza mwambo wapadera pofuna kubweletsa pamodzi anthu ochita malonda m’boma la Likoma.

M’mawu ake mkulu wamalo ogona alendo a Chiponde Beach Resort a Gedion Khuni ati mwambowu ubweletsa pamodzi anthu ochita malonda osiyanasiyana kuphatikizapo mbeu zomwe zimalimadwa m’bomali.

Iwo atinso pamwambowu padzakakhala kupeleka mphoto komanso kugulitsa zinthu zosiyanasiyana monga tomato, masamba, chinangwa komanso malonda ena pamitengo yotsika kusiyana ndi momwe zimagulitsidwira nthawi zonse.

Mwambo omwe akuutcha kuti Farmers Market, udzachitika pa 1 June 2025, ndipo ukachitikira ku Chiponde Beach Resort pomwe oyimba osiyanasiyana akakometsele mwambowu motsogodzedwa ndi Limban Band.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

Kampani ya China Civil Engineering Construction kudzera mu unduna wa za mtengatenga ndi mtokoma yapereka ma life jacket 250 ku boma la Likoma.

Wapampando wa khonsolo ya boma la Likoma wati anthu omwe amapindula ndi porogalamu ya mtukula pakhomo adzigwilitsa moyenera ndalama zomwe amalandila mu porogalamuyi.

Gulu la Tilerane la m’mudzi wa mfumu Mani M’boma la Likoma lathandiza mabanja awiri osowa ndikatundu ogonera.