Mulandu wayemwe akumuganizira kuti ndi m’modzi mwawoyendetsa Boat lomwe linachita ngozi ndikupha anthu nkhumi ndi modzi m’mawa wapa 12 April, 2025, m’boma la Likoma wayamba lero.

Malingana ndi His Worship Fordwatch Nyamazana Mkandawire wati mlanduwu ukuyembekezeka kupitilira lachisanu sabata ino.

Naye otengera milandu ku bwalo lamilandu Sergeant Charles Chilala wati lachisanu abweletsa mboni zawo zonse ndicholinga choti oganizilidwayu asachedwe kuweluzidwa.

Woganizilidwayu ndi a Owen Gondwe ochokera m’boma la Rumphi adzaka 22.

LikomaFM, OnlineNews

Related posts

Khothi la first grade magistrate ku Likoma lagamula a Kingsley Lamwele a zaka 18 kukakhala kundende ndikukagwila ntchito yakalavula gaga kwa zaka zinayi kaamba kolowa m’nyumba ndi kuba katundu osiyanasiyana.

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.