Sukulu ya Likoma Sekondale yalandila galimoto ya tsopano yomwe ikhale ikuchepetsa mavuto a mayendedwe.

Polandila galimotoyi lachinayi m’phunzitsi wamkulu wa pa sukukuyi a Jeremiah Mzumala ati akuthokoza boma kudzera ku nduna yoona za maphunziro a Madalitso Kambauwa Wirima kaamba kokwanilitsa lonjezo lawo.

“anduna azamaphunzilo atabwera pa sukulu yathu mwezi wa epulo chaka chomwechino, tinawadandaulira za vuto la mayendedwe komanso tinawasonyeza galimoto yakale imene tinkakonzetsa pafupipafupi koma simatheka, ndipo kubwera kwa galimoto la tsopanoyi kuchepetsa mavuto ambiri pa sukulu yathu.”

Polankhulapo wapampando wa komiti ya PTA a Anson Putaputa Chirwa anathokoza phungu wa Likoma a Christopher Ashems Songwe poyikapo khama kuti galimotoyi ifike ku Likoma.

“Pakadali pano Budget ichepako kutengela kuti ndalama ina timapeleka kwa akabanza popita kuchipatala ana akadwala, komanso katundu wina tidzithaso kugwiritsa ntchito galimotoyi.” Atero a Putaputa.

LikomaFM,OnlineNews.

Related posts

Mkulu woyang’anira nkhani za katemera wa Polio mdziko muno, a Blessing Nyirongo ati ali ndi chikhulupiliro kuti kampeni yopeleka katemera wamatendawa m’boma la Likoma ikhala yopambana.

Wamkulu wa kampani ya Malawi Lake Services wati kukweza mitengo kwa sitima ya MV Ilala kupititsa patsogolo ntchito za kampaniyi.

Ofesi yowona za usodzi ku Likoma yati ndiyokondwa kuti tsopano asodzi ali ndi owaimira ku khonsolo.

11 comments

Maxwell2701 August 17, 2025 - 10:11 pm
Kendall3605 August 18, 2025 - 6:48 am
Alyssa1356 August 18, 2025 - 11:54 am
Maya658 August 18, 2025 - 12:41 pm
Ivy4822 August 19, 2025 - 2:55 am
Willow1923 August 20, 2025 - 4:56 am
Kara1163 August 20, 2025 - 6:19 am
Lane2003 August 20, 2025 - 10:33 am
Cameron613 August 20, 2025 - 10:52 am
Jared3210 August 22, 2025 - 5:57 pm
Quentin3436 August 24, 2025 - 9:14 am
Add Comment