Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Malingana ndi mneneri wa Police ya Likoma a Andrew Kusimbwa ati kumangidwaku kwachitika pambuyo pa ntchito yomwe inachitika ndi a polisiwa.

“A Banda atiuza kuti anamuuza mwanayo kuti awagwire kumaliseche kwawo, koma mwanayo anakana”

“Iwo akuti anachita zimenezi potsatira malangizo a sing’anga, pokhulupirira kuti mchitidwewu ungamupange kukhala wolemera”, watero Kusimbwa.

A Kusimbwa ati mwanayo anapulumutsidwa ndi amayi ake, omwe anapita kukamufunafuna ataona kuti sanabwerere kunyumba kutsatila kuyitanidwa ndi oganilizidwayu, ndipo amayiwa atafika kunyumba kwa a Banda anapeza zitseko zonse zotsekedwa koma anamva mawu a mwana wawo akufuula kuti athandizidwe.

A Charlse Banda amachokera m’mudzi wa mfumu Mtaya, T.A Mkhumpha m’boma la Likoma ali ndizaka 39 akawonekera kukhoti kuti akayankhe mlandu wochitala mwana zachipongwe.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.

‎kutsatila kutsegulira kwa sukulu pa 22 September chaka chino, gulu la achinyamata lochokera kwa a mfumu a Mani m’mudzi wa Mbungo lapeleka makope ndi zolembera kwa ana apasukulu ya mbungo m’boma la Likoma.‎‎