Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.

A Chilambula amalankhula izi lero pamwambo otsegulira chipatala chaching’ono cha YoMa chomwe chamangidwa m’mudzi wa Yofu m’boma la Likoma.

A Chilambula ati chipatalachi chichepetsa imfa ya ana ang’onoang’ono ndi amayi oyembekezera omwe amafuna thandizo lamsanga komanso chithandizila kuchepetsa matenda.

Polankhulapo wamkulu oyang’anila ntchito za umoyo m’bomali Dr Gracewell Mathewe ati kubwera kwa chipatalachi kusintha zambiri pankhani ya zaumoyo.

“Kutengera ndi level yachipatalachi tidzipereka uphungu kwa amayi oyembekezera, kupereka katemera kwa ana, komanso kuthandiza ngati munthu wavulala mwazina”, atero Dr Mathewe.

Nawo mayi Eneless John ochokera m’mudzi wa mfumu Mnyanje omwe ndiwombekezera pakadali pano ati chipatalachi chichepetsa mtunda omwe amayi oyembekezera amakumana nawo akamapita ku sikelo.

Chipatala cha YoMa chamangidwa ndi ndalama zakwana 146 million kwacha ya thumba la Constituency Development Fund, CDF.

LikomaFM,OnlineNews.

Related posts

Khothi la first grade magistrate ku Likoma lagamula a Kingsley Lamwele a zaka 18 kukakhala kundende ndikukagwila ntchito yakalavula gaga kwa zaka zinayi kaamba kolowa m’nyumba ndi kuba katundu osiyanasiyana.

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.