‎kutsatila kutsegulira kwa sukulu pa 22 September chaka chino, gulu la achinyamata lochokera kwa a mfumu a Mani m’mudzi wa Mbungo lapeleka makope ndi zolembera kwa ana apasukulu ya mbungo m’boma la Likoma.‎‎

M,modzi mwa achinyamata omwe apelereka makopewa a Nick Mkuyamba ati cholinga chachikulu cha gulu lawo ndikupititsa patsogolo maphunziro musukulu za primary m’bomali.‎‎Nawo a Gresham omweso ndi m’modzi mwa achinyamatawa ati achinyamata ali ndi udindo othandiza pachitukuko chadziko munjira zosiyanasiyana.

“makolo ena kapezedwe kawo ndikovutikila ndichifukwa tinaganiza kuti pomwe sukulu zatsegulira titengepo mbali”.

‎M’modzi mwa ana opindula Monica Gama wathokoza achinyamatawa ndipo wati thandizoli limuthandizira kuti maphunziro ake ayende bwino.

‎Achinyamatawa apeleka makope asanu ndi limodzi ndi zolembera ziwiri kwa ana okwana 34.

LikomaFM, OnlineNews.

Related posts

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.

7 comments

Lilly4087 September 28, 2025 - 12:57 am
Davis49 October 9, 2025 - 8:07 am
Steve2417 October 14, 2025 - 1:37 am
Dwight4436 October 27, 2025 - 7:30 am
Erik3794 November 13, 2025 - 9:38 am
Esme4527 December 1, 2025 - 9:54 am
Campbell381 December 2, 2025 - 5:52 am
Add Comment