Khothi la first grade magistrate ku Likoma lagamula a Kingsley Lamwele a zaka 18 kukakhala kundende ndikukagwila ntchito yakalavula gaga kwa zaka zinayi kaamba kolowa m’nyumba ndi kuba katundu osiyanasiyana.

Malingana ndi oyimira boma pa milandu Sub-Inspector Shallnever Mfune adauza khothili kuti usiku wapa 25 July 2026 odandaulayu adatseka nyumba yake koma m’mawa wake anapeza sutikesi ya mdzukulu wake itasowa.

“Sutikesi ndi zinthu zomwe zinali mkati mwake zinali zandalama zokwana 2 million kwacha ndipo zina mwa zinthuzi ndi nsapato, mashati, jazi, mathalauza, yunifolomu za kusukulu, mabulangete komanso 50 sauzande kwacha mwazina”.

First grade magistrate Fordwatch Nyamazana Mkandawire wati wapeleka chilangochi kaamba koti mlandu wakuba katundu wa ophunzira ndi waikulu chifukwa choti umasokoneza maphunziro.

Kingsley Lamwele, amachokera m’mudzi wa Zambala mfumu yaikulu Mwadzama m’boma la Salima.

LikomaFM,OnlineNews.

Related posts

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.