Apolice M’boma la Likoma agwira abambo atatu ndikuwasunga muchitolokosi powaganizira mulandu wakuba komanso kupezeka ndi katundu wa anthu omwe anamira pangozi ya bwato yomwe inachitika loweluka sabata yapitayi m’bomali pomwe anthuwa amakakwera sitima ya MV Chilembwe.

Malingana ndi ofalitsa nkhani za Police ku Likoma sergeant Enala Kaluwa wati pawukadaulo wawo akwanitsa kugwira anthuwa ndipo onsewa akuyembekezeka kukawonekera kubwalo la mulandu posachedwapa pa mlandu opezeka ndi katundu wakuba.

Atatuwa ndi a Sunganani soko
azaka 31 am’mudzi wa Chioko, T.A Nkumpha boma Likoma. Nyangana Nyasulu azaka 32 am’mudzi wa Matandani, T.A Kamwandi boma la Nkhatabay, ndi a Chisomo Ganizani azaka 26 am’mudzi wa Kosamu, T.A Njombwa boma la Kasungu.

Kaluwa wati akwanitsanso kugwira m’modzi mwa anthu omwe amayendetsa bwato lomwe linanyamula anthuwa omwe anamila.

Related posts

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.

‎kutsatila kutsegulira kwa sukulu pa 22 September chaka chino, gulu la achinyamata lochokera kwa a mfumu a Mani m’mudzi wa Mbungo lapeleka makope ndi zolembera kwa ana apasukulu ya mbungo m’boma la Likoma.‎‎