Nthambi yowona zanyengo ndi kusintha kwa nyengo yati mitambo ya mvula ya mabingu yayambapo kale kusonkhana m’madera ena am’dziko muno.

Madelawa ndi monga, Blantyre, Thyolo, Phalombe, Mangochi, Mwanza, Salima mwa ochepa chabe.

Nthambiyi yati izi zikupereka chiyembekezo cha mvula ya mabingu m’maderawa ndi ena ozungulira m’maola angapo akudzawa. Nthambiyi yati mitambo ya mvulayi ikuyembekezeka kufalikiranso m’madera ena ndipo ati tikhale tcheru chifukwa nyengo itha kusintha nthawi ina iliyonse.

Nyengoyi ikupelekanso ziopsezo za mphenzi ndi mvula ya mphamvu choncho tisabisale pansi pamtengo kukamagwa mvula yamabingu.

Related posts

Khothi la first grade magistrate ku Likoma lagamula a Kingsley Lamwele a zaka 18 kukakhala kundende ndikukagwila ntchito yakalavula gaga kwa zaka zinayi kaamba kolowa m’nyumba ndi kuba katundu osiyanasiyana.

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.