Sitima ya MV Chilembwe idziyenda kawiri patsiku kuyambila pa 15 April pakati pa boma la Likoma ndi Nkhata Bay.

“Ndiyankha pompano zokhudza MV Chilembwe zomwe phungu wanyumba ya malamulo wapempha”, nduna yowona za mayendedwe ndi mtengatenga a Jacob Hara ndiwo anena izi pamwambo wotonthoza mabanja omwe akhudzidwa ndi ngozi yabwato yomwe yachitika pa 12 April m’boma la Likoma.

Ndunayi yalamula izi kutsatira pempho la phungu wadelari a Christopher Ashems Songwe.

Related posts

Khothi la first grade magistrate ku Likoma lagamula a Kingsley Lamwele a zaka 18 kukakhala kundende ndikukagwila ntchito yakalavula gaga kwa zaka zinayi kaamba kolowa m’nyumba ndi kuba katundu osiyanasiyana.

Apolisi m’boma la Likoma amanga a Charlse Banda, powaganizira kuti anachita chipongwe msungwana wazaka khumi.

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.