Nthambi yowona zanyengo ndi kusintha kwa nyengo yati mitambo ya mvula ya mabingu yayambapo kale kusonkhana m’madera ena am’dziko muno.

Madelawa ndi monga, Blantyre, Thyolo, Phalombe, Mangochi, Mwanza, Salima mwa ochepa chabe.

Nthambiyi yati izi zikupereka chiyembekezo cha mvula ya mabingu m’maderawa ndi ena ozungulira m’maola angapo akudzawa. Nthambiyi yati mitambo ya mvulayi ikuyembekezeka kufalikiranso m’madera ena ndipo ati tikhale tcheru chifukwa nyengo itha kusintha nthawi ina iliyonse.

Nyengoyi ikupelekanso ziopsezo za mphenzi ndi mvula ya mphamvu choncho tisabisale pansi pamtengo kukamagwa mvula yamabingu.

Related posts

‎kutsatila kutsegulira kwa sukulu pa 22 September chaka chino, gulu la achinyamata lochokera kwa a mfumu a Mani m’mudzi wa Mbungo lapeleka makope ndi zolembera kwa ana apasukulu ya mbungo m’boma la Likoma.‎‎

Mulandu wayemwe akumuganizira kuti ndi m’modzi mwawoyendetsa Boat lomwe linachita ngozi ndikupha anthu nkhumi ndi modzi m’mawa wapa 12 April, 2025, m’boma la Likoma wayamba lero.

Khonsolo ya Likoma yati mwayi wa ntchito zosiyanasiyana ulipo mukhonsoloyi kwa achinyamata omwe ali ndi zowayeneleza.