Nthambi yowona zanyengo ndi kusintha kwa nyengo yati mitambo ya mvula ya mabingu yayambapo kale kusonkhana m’madera ena am’dziko muno.

Madelawa ndi monga, Blantyre, Thyolo, Phalombe, Mangochi, Mwanza, Salima mwa ochepa chabe.

Nthambiyi yati izi zikupereka chiyembekezo cha mvula ya mabingu m’maderawa ndi ena ozungulira m’maola angapo akudzawa. Nthambiyi yati mitambo ya mvulayi ikuyembekezeka kufalikiranso m’madera ena ndipo ati tikhale tcheru chifukwa nyengo itha kusintha nthawi ina iliyonse.

Nyengoyi ikupelekanso ziopsezo za mphenzi ndi mvula ya mphamvu choncho tisabisale pansi pamtengo kukamagwa mvula yamabingu.

Related posts

Wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency a Charles Chilambula ati kubwera kwa incinerator m’boma la Likoma kupititsa patsogolo ntchito za umoyo.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo yemwenso ndi phungu wa Likoma Islands Constituency olemekezeka a Charles Broomhead Chilambula ati boma ndilodzipereka kupititsa patsogolo ntchito zaumoyo.

‎kutsatila kutsegulira kwa sukulu pa 22 September chaka chino, gulu la achinyamata lochokera kwa a mfumu a Mani m’mudzi wa Mbungo lapeleka makope ndi zolembera kwa ana apasukulu ya mbungo m’boma la Likoma.‎‎